Bungwe la Muslim Association of Malawi, lero pa 3 June 2026 lachititsa mkumano wa ma Sheikh komanso anthu ena okhunzidwa.
Cholinga cha mkumanowu kunali kukambirna nkhani zokhunza kulumikizana pakati pa makolo ndi ana pa nkhani ya uchimbere wabwino. Iyi ndi imodzi ya mikumano imene bungwe la Nowergian Church Aid komanso Danish Charch Aid ikuchittsa ndi cholinga chofuna kutolera mbalume zochokera ku mipingo ya mmene makolo angamayankhulanirane ndi ana awo pa nkhani ya uchembere. Potsilinza pa mikumanoyi palembedwa buku lomwe lingakhale ndi ziphunzitso za zipembenzo zosiyanasiyana kumphatikizapo chisilamu.
MAM ndi limodzi mwa mabungwe azipembenzo amene akugwira ntchito yolimbikitsa za uchembere wabwino kwa achinyamata ndipo bungweli likugwira ntchitoyi m' boma la ntchitsi ndi nthandinzo la za chuma lochokera ku Bumgwe la KFW la ku Germany mosogozedwa ndi PSI komanso NCA-DCA kuno ku malawi.
Ena mwa ma sheikh amene anali pa mkumanowu ndi Sh. Muhamad Silka, Sh. Bakar Danken, Sh. Omar Nkachelenga, Sh. Muslim Abass Vinjenje, Sh Swaleh Chilundu ndi ena ambili.